مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه

CHOMBO CHACHIPULUMUTSO

Cover Page
By

Sheikh Salim bin Samayr al-Hadrami

مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 1 · Introduction Yoyamba
⏱️ 20:57
“Kudziwa zokhudza buku li:” Buku li likufotokoza zokhudza ma ibadaat osiyana siyana. Mulibe ma aamalaat ngati zokhudza nikkah, jihaad ndi zina kudzera madh'hab (panjira) ya Imam a Shafi.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 2 · Introduction ya chiwiri
⏱️ 31:24
“Kumulongosola Mulembi:” Introduction ya chiwiri, ikufotokoza zokhudza mulembi, mbiri yake. Uku kukhala kumaliza مقدم (introduction) ya buku li. Izi zimathandiza kwambiri kudziwa bwino zokhudza zomwe zinalembedwa mu book.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 3 · Kudziwa Madhhab ndi Msichi za Chisilamu
⏱️ 32:48
Sheikh anayamba ndikutitambasulira zokhudza madh'hab. Madh'hab si chipembedzo kapena mpingo. Madh'hab ndi njira yomwe ma ُعُلَمَاء (scholars) amagwilitsa tchito kufokotokoza chipembedzo, kuti anthu avetsetse chipembedzo. Kutero sizoletsedwa kwa msilamu kuphuzira madh'hab enaake. Koma kuti, madh'hab safunika kuwatsatira mwa umbuli kufika pomatsutsa Qur'an ndi ma hadith a swahih kamba kotsatira madh'hab.
مَنْ يُرِدِ اللّٰهُ بِهِ خَيْراً يُفَقِّهْهُ فِي الدِّينِ (Amene Allah angamufunire zabwino, amampatsa kunvetsa chipembedzo). Zili zabwino kwa msilamu kuti akamayamba zinazake adziyamba ndikumuyamika Allah. Izi sitikuyenera kumazipanga ku zithu za deen zokha iyayi, ngakhale za duniyah zimafunika kumampempha chithandizo Allah (سبحانه وتعالى) kuti zitiyendere bwino.
Sheikh, anayamba ndi kutipatsira khomo la msichi za Chisilamu (ِأَرْكَانُ الْإِسْلَام). China chilichonse chokhudza Chisilamu chinagona kapena Kutuluka mu msichi 5 zomwe ndi ku: 1. Kukhulupira kuti palibe wina oyenera kupembedzedwa koma Allah ekha komanso Muhammad ndi Mtumiki wa Allah. 2. Kuimika swalah 3. Kupereka zakah 4. Kusala mmwezi wa Ramadhan 5. Kupita ku Hajj kwa amene Allah wamufewetsera
Asilamu tiyeni tiphunzire kuti tidziwe komanso kuvetsetsa chipembedzo chi. Izi zithandiza kubweretsa umodzi pakati pathu.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 4 · Msichi za Iman
⏱️ 25:16
“Msichi za chikhulupiliro (Imaan), ِأَرْكَانُ الْإِيْمَان:” Msichi za Chisilamu ndizosiyana ndi msichi za imaan. Asilamu, dziwani kuti ngati munthu angapange kapena kukwanilitsa msichi za Chisilamu opanda imaan, zikhalama zopanda zipatso.
Msichi za imaan zilipo 6 Kukhulupilira mwa; 1. Allah 2. Angelo ake 3. Mmabuku ake 4. Atumiki ake 5. Tsiku lomaliza 6. Mu mchikozero chabwino komanso choyipa zimachokera kwa Iye, Allah
Tinaonaso gawo la tathauzo la tauhid. Tauhid ndi kukhulupilira kuti palibe wina opembedzedwa mwa choonadi koma Allah ekha basi, لَا إِلٰهَ إِلَّا اللّٰهُ. Tiyenera Kudziwa kuti, kuti tipindure ndi لَا إِلٰهَ إِلَّا اللّٰهُ, tiyenera kudziwa bwino bwino zokhudza mawu amenewa. Koma ngati tingapange chidule ponyalanyaza kudziwa kapena kuphuzira tathauzo lake, ndithu tidzakhala osochera ndi otayika. Asilamu ambiri ngati akupanga zinthu molakwika ndi kamba koti sananvetse bwino tathauzo la لَا إِلٰهَ إِلَّا اللّٰهُ. Allah atiteteze kuzimenezi.
Munthu ayenera kudziwa ndi kutsimikiza zoti palibe wina opembedzedwa koma Allah ekha kuyambira mumtima mwake, kenako alakhule ndi lilime lake ndipo ziwalo zake zitsatire pogwira tchito yopembedza Allah ekha yo basi.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 5 · Zizindikiro za kutha Msikhu
⏱️ 36:06
“Zizindikiro zakutha msinkhu, عَلَامَاتُ الْبُلُوغِ.:” Ndi zofunika kuti msilamu adziwe zizindikiro za kutha msinkhu chifukwa malumulo a Chisilamu amayamba kugwira tchito pa munthu pamene wakula. Mtumiki anati: "رُفِعَ الْقَلَمُ عَنْ ثَلَاثَةِ ", tathauzo: "Cholembera chimanyamulidwa kwa anthu atatu". Kutathauza kuti Angelo samalemba machimo a anthu atatu. Mmodzi mwa iwo ndi mwana mpaka atatha msinkhu, ْعَن الصَّبِيِّ حَتَّى يَحْتَلِمَ.
Zizindikiro zakutha msinkhu zilipo zitatu: 1. Kukwanitsa zaka 15 2. Kudzilotera kwa munthu amene wafika zaka 9 3. Kusamba kwa munthu wa mkazi amene wafika zaka 9
Tikamakamba za mthawi ku sharia (malumulo a Chisilamu), timagwiritsa tchito hijri calendar (ya Chisilamu) chifukwa imasiyana ndi Gregorian calendar (Yomwe timagwiritsa tchito kwathu kuno).
Komanso tidziwe kuti zizindikiro zi sizikufunika kuti zonse zikumane pakamodzi. Kupezeka kwa chimodzi mwa zizindikiro zimenezi kumakwanira kuti mwana watha msinkhu, wakula.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 6 · Kupeza twahara pogwiritsa tchito mwala
⏱️ 33:42
“Kugwiritsa tchito mwala, tissue ndi zina podziyeretsa, ُالْاِسْتِنْجَاء:” Kudziwa mmene tikuyenerera kudziyeretsera ndi zofunika kwambiri kwa Msilamu chifukwa pali zinthu zina ngati swalah komanso ma ِعِبَادَات ena omwe tikuyenera kupanga tili ndi twahara, oyera.
Sheikh anatidziwitsa za malamulo amene amayenereza kugwiritsa tchito mwala popanga istin'jaai, ُالْإِسْتِنْجَاء. Istin'jaa, njira yochotsera nyasi pogwiritsa tchito madzi, ndi njira yoyamba yodziyeretsera, first priority. Pamene Istijmaar, njira yochotsera nyasi pogwiritsa tchito mwala ndi zina zolowa mmalo mwa mwala, ndi njira ina yodziyeretsera, second priority.
Njira yogwiritsa tchito mwala, inabwera kamba kofuna kupeputsa chipembedzo ndipo ndi yokwanira payokha posagwiritsanso tchito madzi pambuyo pogwiritsa tchito mwala. Komanso, mwala kapena zolowa mmalo mwake zikhoza kugwiritsidwa tchito angakhale madzi alipo. Zinthu zomwe ndi najsi kapena zili ndi najsi sizoyenera kugwiritsidwa tchito podziyeretsa.
Zinthu zimene zingagwiritsidwe tchito ngati mwala pochotsera nyasi, ُنَجْس, zikuyenera kukhala ndi zithu 4: 1. Chikhale chowuma, chosanyowa 2. Chikhale cha twahara, choyera 3. Chikhale ndikhuthekera kochotsa najsi 4. Chisakhale chinthu cholemekezeka
Tidziwe kuti kusowekera kwa chinthu chimodzi mu zinthu zoyenereza kugwiritsa tchito mwala pochotsa nyasi, kumampangitsa munthu kuti abwerere kogwiritsa tchito madzi.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 7 · Malamulo amene amayenereza kugwiritsa tchito mwala
⏱️ 30:50
“Malamulo amene amayenereza kugwiritsa tchito mwala popanga istinjaa, ِشُرُوطُ إِجْرَاء الْحَجَرِ فِي الْاِسْتِنْجَاءِ:” Ndizofunikira kuti tidziwe kuti instijaa ili ndi malamulo ake okwana 5: 1. Zokakamiza munthu kupanga istinjaa 2. Zabwino kukapanga istinjaa 3. Zololezedwa chabe kukapanga istinjaa 4. Zonyasa kukapanga istinjaa 5. Zoletsedwa kukapanga istinjaa
Najsi (نَجْسُ) ndi nyasi kapena chilichonse cha unve. Malumulo amene amayenereza kugwiritsa tchito mwala popanga istinjaa alipo 8: 1. Ikuyenera kukhala miyala itatu 2. Miyalayo kapena cholowa mmalo mwa mwala chikuyenera kukhala ndi kuthekera kuchotsa najsi 3. Najsi sikuyenera kukhala yowuma 4. Najsi sikuyenera kusamuka ndi kugunda mbali ina yathupi 5. Sipakuyenera kubwera najsi ina pamwamba pa najsi yo 6. Najsi sikuyenera kuyenderera mpaka kugunda mmatako 7. Najsi yo isagundindwe ndi madzi 8. Miyala yopangira istinjaa ikhale yoyera
Tidziwe kuti, kusowekera kwa chimodzi mwa izi, mzimakhala zokamazikika kuti munthu agwiritse tchito madzi pochotsa najsi.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 8 · Zikakamizo za pa wudhu
⏱️ 33:14
“zinthu zichikakamizo popanga wudhu, ِفَرَائِضُ الْوُضُوْء:” Ma عُلَمَاءُ, scholars, a madh'hab a Shafi anaugawa wudhu mu ma gawo awiri; 1. Zinthu zachikakamizo pa wudhu 2. Zinthu zomwe zili sunnah pa wudhu
Tidziweso kuti kavedwe komati pali wudhu wa فَرَضٌ (wachikakamizo) ndi wa سُنَّةٌ (sunnah) ndi kolakwika chifukwa, zimatathauza kuti ngati tingasiye osapanga wudhu wa chikakamizo ndeti wudhu wathu sunatheke.
Zinthu zimene zili zachikakamizo kupanga pa wudhu zilipo 6: 1. Chitsimikizo النِّيَةُ 2. Kusambitsa kukhope 3. Kusambitsa mmanja awiri mpaka mkasukusuku 4. Kupukuta pa mutu 5. Kusambitsa miyendo iwiri 6. Kupanga mwa ndondomeko التَّرْتِيبُ
Asilamu tidziwe kuti wudhu ndi chinthu chofunikira kwambiri chifukwa ndi chinthu chimodzi chomwe chimafufuta machimo a munthu wopanga yo komanso ndi chitetezo ku zinthu zonyasa monga ziwanda (ma jinn). Ngati tingapange wudhu mosasamala komanso mwa umbuli ndeti sitidzapeza ma phindu ake komanso tidzakhala ndi chilango.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 9 · Kufokotokoza za wudhu, chitsimikizo ndi ndondomeko
⏱️ 26:19
“Kupitiliza kufokotokozera wudhu:” Tikumbutsane kuti paja buku lomwe tikuphuzitsana li, linalembedwa ndi Madh'hab a Shaffie. Kumbali ya wudhu, madh'hab Shaffie anawugawa wudhu mmagawo awiri amene tinabweretsa mu lesson 8 aja kuti; "Zinthu zachikakamizo pa wudhu" ndi "Zinthu za sunnah pa wudhu". Komanso anatibweretsera zithu 6 zomwe zili zachikakamizo pa wudhu. Kutathauza kuti zinthu zomwe sanazibweretse mu zinthu 6 zi, madh'hab a Shaffie anazitenga kuti ndiza Sunnah, monga;
  • Kutsuka mkamwa ndi mphuno, المضمضة و الاستنشاق.
  • Kusambitsa kepena kutsuka ziwalo katatu
  • Kupukuta mmakutu

Kutengera kuti maphunziro anthu sali limited ku za madh'hab a modzi komanso kukana kutsatira madh'hab mwa umbuli. Madh'hab ena komanso ma عُلَمَاءُ (scholars) ena, samawugawa wudhu mmagawo awiri. Kutathauza kuti amangoika kuti wudhu ndi umodzi basi kutengera ndi ma umboni ochokera kwa Mtumiki wathu (ﷺ) kuti sanawugawe wudhu mmagawo awiriwa komanso sanasiyeko osatsuka mkamwa ndi mphuno ndi kupukuta pa mmakutu.
Madh'hab ena ndi ma Ulamaa anawunikiranso kuti pamene Allah watilamula kusukusula ku maso (فَاغْسِلُوا وُجُوهَكُمْ), nkhope singakhale nkhope opanda pakamwa ndi mphuno. Kutathauza kuti pakamwa ndi mphuno ndi mbali imodzi ya nkhope. Chimodzimodzi, kupukuta makutu zili pamodzi ndi kupukuta pa mutu, وَامْسَحُوا بِرُءُوسِكُمْ, chifukwa makutu ndi mbali imodzi ya mutu.
Pa chifukwa ichi, zabwino kwambiri ndi kusawugawa wudhu mmagawo awiri. Izi ndi zomwe zili chifupi ndi chilungamo.
“Kupitiliza kufokotokozera wudhu kumbali ya Chitsimikizo ndi ndondomeko, ِفِي النِّيَّة وَالتَّرْتِيبِ:” Chitsimikizo (النِّيَّةُ) ndi kutsimikiza kulikonse pofuna kupanga chinthu. Munthu utha kupanga niyyah mthawi ina iliyonse potengera kufotokoza kwa ma ulama pa zomwe zili chifupi ndi chilungamo. Niyyah malo ake ndi mumtima, مَحَلُّهَا الْقَلْبُ, chifukwa mtima ndi omwe umasiyanitsa zinthu pakati popanga zinthu mwa chikhalidwe ndi kupembedza, عَادَ وَعِبَادَة. Choncho ndizosayenera kulakhula niyyah ndi lilime pomwe tikufuna kupanga tchito yopembedza ina iliyonse. Izi ndi zomwe zili chifupi ndi chilungamo chifukwa ma عُلَمَاءُ ena anati "التَّلَفُّظُ بِهَا بِدْعَة", kuyiyakhula niyyah ndi lilime ndizopeka.
Kulondoloza popanga wudhu, التَّرْتِيْبُ, kumathauza kuti kuyambira kumaso, kenako mmanja, kenako pa mutu ndikumalizira miyendo. Choncho sizoyenera kuyamba kusambitsa miyendo kapena manja usanasukusule kumaso.
مَتْنُ سَفِيْنَةِ النَّجَاه Lesson 10 · Mu malamulo a madzi
⏱️ 30:44
“Gawo la mu malamulo a madzi, فِي أَحْكَامِ الْمَاءِ:” Kudziwa za madzi ndi chinthu chofunika chifukwa madzi ndi chinthu chimodzi chomwe timagwiritsa tchito kupezera twahara.
Mulembi anatidziwitsa za madzi kudzera mmagulu awiri, Madzi ochepa ndi ochuluka, الْمَاءُ قَلِيلٌ وَكَثِيرٌ. Madzi amawonengeka twahara yake pa kusintha mu zinthu zitatu; 1. Fungo, رِيحٌ 2. Mtundu, لَوْنٌ 3. Taste, طَعْمٌ
Madzi ochepa ndi omwe sanafike 200 liters, قُلَّتَينِ. Madzi ochepa amakhala a najsi ngati mwagwera najsi angakhale madziwo sanasinthe mu zithu zitatu zi.
Madzi ambiri ndi omwe adutsa 200 liters. Madzi ambiri samawonongeka twahara yake ndi kugweramo najsi kungopatula ngati atasintha mtundu, fungo, ndi taste yake.
Izi ndi zomwe mulembi anatipatsira zokhudza madzi kudzera pa madh'hab a Imam Shafi.
Mtumiki (ﷺ), anati: "إِنَّ الْمَاءَ طَهُورٌ لَا يُنَجِّسُهُ شَيْءٌ", tathauzo: "Ndithu madzi ndi oyera ndipo palibe chomwe chingawaipitse". Ma ulama anatambasula kuvetsetsa izi kuti madzi ngati anali a bwinobwino samakhala a najsi, ochepa olo ochuluka, kungopatula ngati mutagwera najsi yomwe ingasinthe mtundu, fungo, ndi taste ya madziwo. هَذَا قَرِيبُ مِنَ الْصِدْقِ, Izi ndi zomwe zili chifupi ndi chilungamo.