“Kupitiliza kufokotokozera wudhu:”
Tikumbutsane kuti paja buku lomwe tikuphuzitsana li, linalembedwa
ndi Madh'hab a Shaffie. Kumbali ya wudhu, madh'hab Shaffie
anawugawa wudhu mmagawo awiri amene tinabweretsa mu lesson 8 aja
kuti; "Zinthu zachikakamizo pa wudhu" ndi "Zinthu za sunnah pa
wudhu". Komanso anatibweretsera zithu 6 zomwe zili zachikakamizo
pa wudhu. Kutathauza kuti zinthu zomwe sanazibweretse mu zinthu 6
zi, madh'hab a Shaffie anazitenga kuti ndiza Sunnah, monga;
- Kutsuka mkamwa ndi mphuno, المضمضة و الاستنشاق.
- Kusambitsa kepena kutsuka ziwalo katatu
- Kupukuta mmakutu
Kutengera kuti maphunziro anthu sali limited ku za madh'hab a
modzi komanso kukana kutsatira madh'hab mwa umbuli. Madh'hab ena
komanso ma عُلَمَاءُ (scholars) ena, samawugawa wudhu mmagawo
awiri. Kutathauza kuti amangoika kuti wudhu ndi umodzi basi
kutengera ndi ma umboni ochokera kwa Mtumiki wathu (ﷺ) kuti
sanawugawe wudhu mmagawo awiriwa komanso sanasiyeko osatsuka
mkamwa ndi mphuno ndi kupukuta pa mmakutu.
Madh'hab ena ndi ma Ulamaa anawunikiranso kuti pamene Allah
watilamula kusukusula ku maso (فَاغْسِلُوا وُجُوهَكُمْ), nkhope
singakhale nkhope opanda pakamwa ndi mphuno. Kutathauza kuti
pakamwa ndi mphuno ndi mbali imodzi ya nkhope. Chimodzimodzi,
kupukuta makutu zili pamodzi ndi kupukuta pa mutu, وَامْسَحُوا
بِرُءُوسِكُمْ, chifukwa makutu ndi mbali imodzi ya mutu.
Pa chifukwa ichi, zabwino kwambiri ndi kusawugawa wudhu mmagawo
awiri. Izi ndi zomwe zili chifupi ndi chilungamo.
“Kupitiliza kufokotokozera wudhu kumbali ya Chitsimikizo ndi
ndondomeko, ِفِي النِّيَّة وَالتَّرْتِيبِ:”
Chitsimikizo (النِّيَّةُ) ndi kutsimikiza kulikonse pofuna kupanga
chinthu. Munthu utha kupanga niyyah mthawi ina iliyonse potengera
kufotokoza kwa ma ulama pa zomwe zili chifupi ndi chilungamo.
Niyyah malo ake ndi mumtima, مَحَلُّهَا الْقَلْبُ, chifukwa mtima
ndi omwe umasiyanitsa zinthu pakati popanga zinthu mwa chikhalidwe
ndi kupembedza, عَادَ وَعِبَادَة. Choncho ndizosayenera kulakhula
niyyah ndi lilime pomwe tikufuna kupanga tchito yopembedza ina
iliyonse. Izi ndi zomwe zili chifupi ndi chilungamo chifukwa ma
عُلَمَاءُ ena anati "التَّلَفُّظُ بِهَا بِدْعَة", kuyiyakhula
niyyah ndi lilime ndizopeka.
Kulondoloza popanga wudhu, التَّرْتِيْبُ, kumathauza kuti
kuyambira kumaso, kenako mmanja, kenako pa mutu ndikumalizira
miyendo. Choncho sizoyenera kuyamba kusambitsa miyendo kapena
manja usanasukusule kumaso.